1Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira,Ine sindileka kuwalanga.Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu,mpaka kuwasandutsa phulusa,
2Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu,umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti.Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa,mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.
3Ndidzawononga wolamulira wakendi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,”akutero Yehova.
4Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira,Ine sindileka kuwalanga.Popeza iwo akana lamulo la Yehovandipo sanasunge malangizo ake,popeza asocheretsedwa ndi milungu yabodza,milungu imene makolo awo ankayitsatira,
5Ine ndidzatumiza moto pa Yuda,umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu.”
6Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Israeli akunka nachimwirachimwira,Ine sindileka kuwalanga.Iwo amagulitsa anthu olungama ndi siliva,ndi osauka ndi nsapato.