9Anawukoka ndi ngowe nawuponya mʼchitatanga.Anabwera nawo kwa mfumu ya ku Babulonindipo mfumuyo inawuponya mʼndendendi cholinga choti liwu lake lisamamvekensoku mapiri a Israeli.
9
10“ ‘Amayi ako anali ngati mpesa mʼmunda wamphesawodzalidwa mʼmbali mwa madzi.Unabereka bwino ndipo unali ndi nthambi zambirichifukwa cha kuchuluka kwa madzi.
11Nthambi zake zinali zolimba,zoyenera kupangira ndodo yaufumu.Unatalika nusomphoka pakati pazomera zina.Unkaoneka bwino chifukwa cha kutalika kwake,ndi nthambi zake zambiri.
12Koma unazulidwa mwaukalindipo unagwetsedwa pansi.Unawuma ndi mphepo ya kummawa,zipatso zake zinayoyoka;nthambi zake zolimba zinafotandipo moto unapsereza mtengo wonse.
13Ndipo tsopano anawuwokeranso ku chipululu,dziko lowuma ndi lopanda madzi.
14Moto unatulukanso mu mtengomondi kupsereza nthambi ndi zipatso zake.Palibe nthambi yolimba inatsala pa mtengowoyoyenera kupangira ndodo yaufumu.
14Imeneyi ndi nyimbo yachisoni ndipo yasanduka nyimbo ya pa maliro.’ ”