2“Iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuwuza dziko la Israeli kuti:
2“Chimaliziro! Chimaliziro chafikaku ngodya zinayi za dziko.
3Chimaliziro chili pa iwe tsopano.Mkwiyo wanga ndidzawuthira pa iwe.Ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe akondi kukulanga chifukwa cha zonyansa zako.
4Ine sindidzakumvera chisonikapena kukuleka.Ndidzakulanga ndithu chifukwa cha ntchito zako zoyipakomanso chifukwa cha miyambo yako yonyansa imene ili pakati pako.
4Pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
5“Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: “Chiwonongeko! Chiwonongeko chimene sichinamvekepo!Taona chikubwera!
18Iwo adzavala zigudulindipo adzagwidwa ndi mantha.Adzakhala ndi nkhope zamanyazindipo mitu yawo adzameta mpala.
18
19“Iwo adzataya siliva wawo mʼmisewundipo golide wawo adzakhala chinthu chonyansa.Siliva ndi golide wawosizidzatha kuwapulumutsapa tsiku la ukali wa Yehova.Chuma chawochi sichidzawathandiza kuthetsa njala,kapena kukhala okhuta,pakuti ndicho chinawagwetsa mʼmachimo.
20Iwo ankanyadira zodzikongoletsera zawo zamakakandipo ankazigwiritsa ntchito kupanga mafano awo onyansa ndi zonyansa zawo zina.Nʼchifukwa chake Ine ndidzazisandutsakukhala zowanyansa.
21Ndidzazipereka kwa alendo kuti azifunkhe.Anthu oyipa a dziko lapansi adzazilandandi kudziyipitsa.
22Ine ndidzawalekerera anthuwondipo adzayipitsa malo anga apamtima.Adzalowamo ngati mbalandi kuyipitsamo.
23“Konzani maunyolo, chifukwa dziko ladzaza ndi anthu opha anzawondipo mzinda wadzaza ndi chiwawa.
24Ndidzabweretsa mitundu ya anthu oyipitsitsakuti idzalande nyumba zawo.Ndidzathetsa kunyada kwa anthu amphamvupamene anthu akunja adzalowa mʼmalo awo achipembedzo ndi kuyipitsamo.
25Nkhawa ikadzawafikiraadzafunafuna mtendere koma osawupeza.
26Tsoka lidzatsatana ndi tsoka linzake,ndipo mphekesera idzatsatana ndi mphekesera inzake.Iwo adzayesa kufuna masomphenya kuchokera kwa mneneri.Adzasowa ansembe owaphunzitsa malamulo,ndipo anthu akuluakulu sadzakhalanso ndi uphungu.
27Mfumu idzalira,kalonga adzagwidwa ndi mantha.Manja a anthu a mʼdzikomo azidzangonjenjemera ndi mantha.Ine ndidzawalanga molingana ndi machitidwe awo,ndipo ndidzawaweruza molingana ndi momwe anaweruzira anzawo.