1Inu Aisraeli, imvani mawu a Yehova,chifukwa Yehova ali ndi mlandu ndi inuamene mumakhala mʼdzikoli:“Mʼdziko mwanu mulibe kukhulupirika, mulibe chikondimulibe kulabadira za Mulungu.
2Muli kutemberera kokha, kunama ndi kupha.Kuba ndi kuchita chigololo;machimo achita kunyanyandipo akungokhalira kuphana.
3Chifukwa chake dziko likulirandipo onse amene amakhalamo akuvutika;zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalengandiponso nsomba zamʼnyanja zikufa.
3
4“Koma wina asapeze mnzake chifukwa,wina aliyense asayimbe mlandu mnzake,pakuti anthu ako ali ngati anthuamene amayimba mlandu wansembe.
6“Pakuti mwakana kudziwa, Inenso ndidzakukanani monga ansembe anga;chifukwa mwayiwala lamulo la Mulungu wanu,Inenso ndidzayiwala ana anu.
7Ansembe ankati akachulukaiwo ankandichimwiranso kwambiri;iwo anasinthanitsa ulemerero wawo ndi chinthu china chonyansa.
8Amalemererapo pa machimo a anthu angandipo amafunitsitsa kuti anthuwo azipitiriza kuchimwa.
9Ndipo zidzakhala motere: zochitikira anthu ena, zidzachitikiranso ansembe.Ndidzawalanga onsewo chifukwa cha njira zawo,ndidzawabwezera chifukwa cha machitidwe awo.
9
10“Iwo azidzadya koma sadzakhuta;azidzachita zachiwerewere koma sadzachulukana,chifukwa anasiya Yehovakuti adzipereke
11ku zachiwerewere,ku vinyo wakale ndi watsopano,zimene zimachotsa nzeru zomvetsa zinthu
12za anthu anga.Anthu anga amapempha nzeru ku fano lamtengondipo ndodo yawo yamtengo imawayankha.Mzimu wachiwerewere umawasocheretsa;iwo sakukhulupirika kwa Mulungu wawo.
13Amapereka nsembe pamwamba pa mapirindi kufukiza lubani pa zitunda,pa tsinde pa mtengo wa thundu, mnjale ndi mkundi,pamene pali mthunzi wabwino.Nʼchifukwa chake ana anu aakazi akuchita zachiwerewerendipo akazi a ana anu akuchita zigololo.
13
14“Ine sindidzalanga ana anu aakazipamene iwo adzachita zachiwerewere,kapena akazi a ana anupamene adzachita zigololo.Paja inu nomwe amunanu mumayenda ndi akazi achiwerewere,ndipo mumapereka nsembe pamodzi ndi akazi achiwerewere a ku malo opembedzerako.Anthu amene alibe nzeru adzawonongeka ndithu!
14
15“Ngakhale umachita chigololo, iwe Israeli,Yuda asapezeke ndi mlandu wotere.
15“Usapite ku Giligala. Usapite ku Beti-Aveni.Ndipo usalumbire kuti, ‘Pali Yehova wamoyo!’
16Aisraeli ndi nkhutukumve,ngosamva ngati ana angʼombe.Kodi Yehova angathe kuwaweta bwanjingati ana ankhosa pa msipu wabwino?