Masalimo 113:1-9 NYCCL2016 - Bible AI

1Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.

2Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.

3Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.

3

4Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.

5Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?

6amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?

6

7Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;

8amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.

9Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala.

9Tamandani Yehova.

e>