Masalimo 114:1-8 NYCCL2016 - Bible AI

1Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,

2Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.

2

3Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;

4mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.

4

5Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?

6inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?

6

7Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,

8amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.

e>