1Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
2Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
2
3Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
4Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
4
5Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
6Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
7Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.