Masalimo 124:1-8 NYCCL2016 - Bible AI

1Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, anene tsono Israeli,

2akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, potiwukira anthuwo,

3iwo atatipsera mtima, akanatimeza amoyo;

4chigumula chikanatimiza, mtsinje ukanatikokolola,

5madzi a mkokomo akanatikokolola.

5

6Atamandike Yehova, amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.

7Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame yokodwa mu msampha wa mlenje; msampha wathyoka, ndipo ife tapulumuka.

8Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

e>