Masalimo 127:1-5 NYCCL2016 - Bible AI

1Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni. Yehova akapanda kumanga nyumba, omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe. Yehova akapanda kulondera mzinda, mlonda akanangolondera pachabe.

2Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa ndi kusagona msanga madzulo, kuvutikira chakudya choti mudye, pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.

2

3Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova, ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.

4Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja mwa munthu wankhondo.

5Wodala munthu amene motengera mivi mwake mwadzaza. Iwo sadzachititsidwa manyazi pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.

e>