Masalimo 128:1-6 NYCCL2016 - Bible AI

1Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.

2Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.

3Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.

4Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.

4

5Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,

6ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako.

6Mtendere ukhale ndi Israeli.

e>