1Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,” anene tsono Israeli;
2“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga, koma sanandipambane.
3Anthu otipula analima pa msana panga ndipo anapangapo mizere yayitali:
4Koma Yehova ndi wolungama; Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
4
5Onse amene amadana ndi Ziyoni abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
6Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba, umene umafota usanakule;
7sungadzaze manja a owumweta kapena manja a omanga mitolo.
8Odutsa pafupi asanene kuti, “Dalitso la Yehova lili pa inu; tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”