Masalimo 137:1-9 NYCCL2016 - Bible AI

1Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.

2Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,

3pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”

3

4Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?

5Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.

6Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.

6

7Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”

7

8Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.

9Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.

e>