1Tamandani Yehova. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, matamando ake mu msonkhano wa oyera mtima.
2Israeli asangalale mwa mlengi wake; anthu a ku Ziyoni akondwere mwa Mfumu yawo.
3Atamande dzina lake povina ndi kuyimbira Iye nyimbo ndi tambolini ndi pangwe.
4Pakuti Yehova amakondwera ndi anthu ake; Iye amaveka chipulumutso odzichepetsa.
5Oyera mtima asangalale mu ulemu wake ndi kuyimba mwachimwemwe pa mabedi awo.
5
6Matamando a Mulungu akhale pakamwa pawo, ndi lupanga lakuthwa konsekonse mʼmanja mwawo,
7kubwezera chilango anthu a mitundu ina, ndi kulanga anthu a mitundu yonse,
8kumanga mafumu awo ndi zingwe, anthu awo otchuka ndi unyolo wachitsulo,
9kuchita zimene zinalembedwa zotsutsana nawo Uwu ndi ulemerero wa oyera mtima ake onse.