4Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova,ichi ndi chimene ndidzachifunafuna:kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehovamasiku onse a moyo wanga,ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova,ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.
5Pakuti pa tsiku la msautsoIye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo;adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yakendi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.
6Kotero mutu wanga udzakwezedwakuposa adani anga amene andizungulira;pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe;ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.