1Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide.Chitsiru chimati mu mtima mwake,“Kulibe Mulungu.”Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa;palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.
2Mulungu kumwamba amayangʼana pansi panopa ana a anthukuti aone ngati alipo wina wanzeru,wofunafuna Mulungu.
5Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulupamene panalibe kanthu kochititsa mantha.Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo;inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.
5
6Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni!Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake,lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!