1Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo.Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa,achititse kuti nkhope yake itiwalire.
2Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi,chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
2
3Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
4Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe,pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamondi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
5Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.