4Ife ndife chinthu chonyozeka kwa anansi athu,choseketsa ndi cholalatiridwa kwa iwo amene atizungulira.
4
5Mpaka liti Inu Yehova? Kodi mudzakwiya mpaka muyaya?Kodi mpaka liti nsanje yanu idzayaka ngati moto?
6Khuthulirani ukali wanu pa anthu a mitundu inaamene sakudziwani Inu,pa maufumuamene sayitana pa dzina lanu;
7pakuti iwo ameza Yakobondi kuwononga dziko lawo.
8Musatilange chifukwa cha machimo a makolo athuchifundo chanu chibwere msanga kukumana nafe,pakuti tili ndi chosowa chachikulu.
8
9Tithandizeni Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu;tipulumutseni ndi kutikhululukira machimo athuchifukwa cha dzina lanu.
10Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akuti,“Ali kuti Mulungu wawo?”Ife tikuona, zidziwike pakati pa anthu a mitundu inakuti mumabwezera chilango chifukwa cha magazi amene anakhetsedwa a atumiki anu.
11Kubuwula kwa anthu a mʼndende kufike pamaso panu;ndi mphamvu ya dzanja lanumuwasunge amene aweruzidwa kuti aphedwe.
11
12Mubwezere kwa anansi athu kasanu nʼkawirikunyoza kumene ananyoza Inu Ambuye.
13Pamenepo ife anthu anu, nkhosa za pabusa panu,tidzakutamandani kwamuyaya,kuchokera mʼbado ndi mʼbadotidzafotokoza za matamando anu.