1Salimo la Asafu. Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
2“Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa?
3Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
4Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
4
5“Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
5
6“Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
7Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
7
8Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.