1Salimo la Ana a Kora. Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;
2Yehova amakonda zipata za Ziyoni kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.
3Za ulemerero wako zimakambidwa, Iwe mzinda wa Mulungu: Sela
4“Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni pakati pa iwo amene amandidziwa. Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi, ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’ ”
4
5Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti, “Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye, ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”
6Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina: “Uyu anabadwira mʼZiyoni.” Sela
7Oyimba ndi ovina omwe adzati, “Akasupe anga onse ali mwa iwe.”