1 Buku lofotokoza za mʼbado wa Yesu Khristu mwana wa Davide, mwana wa Abrahamu:
2 Abrahamu anabereka Isake, Isake anabereka Yakobo, Yakobo anabereka Yuda ndi abale ake.
3 Yuda anabereka Perezi ndi Zara, amene amayi awo anali Tamara. Hezironi anabereka Aramu.
3 Perezi anabereka Hezironi,
4 Aramu anabereka Aminadabu, Naasoni anabereka Salimoni.
4 Aminadabu anabereka Naasoni,
5 Salimoni anabereka Bowazi amene amayi ake anali Rahabe, Obedi anabereka Yese.
5 Bowazi anabereka Obedi amene amayi ake anali Rute,
6 Yese anabereka Mfumu Davide.
6 Ndipo Davide anabereka Solomoni, amene amayi ake anali mkazi wa Uriya.
7 Solomoni anabereka Rehabiamu, Abiya anabereka Asa,
7 Rehabiamu anabereka Abiya,
8 Asa anabereka Yehosafati, Yoramu anabereka Uziya.
8 Yehosafati anabereka Yoramu,
9 Uziya anabereka Yotamu, Ahazi anabereka Hezekiya.
9 Yotamu anabereka Ahazi,
10 Hezekiya anabereka Manase, Amoni anabereka Yosiya.
10 Manase anabereka Amoni,
11 Yosiya anali atabala Yekoniya ndi abale ake pamene Ayuda anatengedwa ukapolo kupita ku Babuloni.
11
12 Ali ku ukapolo ku Babuloni, Salatieli anabereka Zerubabeli.
12 Yekoniya anabereka Salatieli,
13 Zerubabeli anabereka Abiudi, Eliakimu anabereka Azoro.
13 Abiudi anabereka Eliakimu,
14 Azoro anabereka Zadoki, Akimu anabereka Eliudi.
14 Zadoki anabereka Akimu,
15 Eliudi anabereka Eliezara, Matani anabereka Yakobo.
15 Eliezara anabereka Matani,
16 Yakobo anabereka Yosefe, mwamuna wa Mariya. Mariyayu ndiye anabereka Yesu wotchedwa Khristu.
17 Kuyambira pa Abrahamu mpaka pa Davide, pali mibado khumi ndi inayi. Ndipo kuyambira pa Davide mpaka pamene Ayuda anatengedwa kupita ku ukapolo ku Babuloni, pali mibado khumi ndi inayi. Ndiponso kuyambira nthawi ya ukapolo ku Babuloni mpaka pamene Khristu anabadwa, palinso mibado khumi ndi inayi.
18 Kubadwa kwa Yesu Khristu kunali motere: Amayi ake, Mariya, anapalidwa ubwenzi ndi Yosefe, koma asanagone malo amodzi, anapezeka ali woyembekezera mwana mwa mphamvu ya Mzimu Woyera.
19 Popeza Yosefe mwamuna wake anali munthu wolungama, sanafune kumuchititsa manyazi pomuleka poyera. Choncho anaganiza zomuleka mosaonetsera.
20 Koma akuganiza zimenezi, taonani, mngelo wa Ambuye anamuonekera mʼmaloto nati, “Yosefe mwana wa Davide, usaope kumutenga Mariya kukhala mkazi wako, chifukwa mwana akuyembekezerayo ndi wochokera kwa Mzimu Woyera.
21 Ndipo adzabala mwana wamwamuna, udzamutcha dzina lake Yesu; pakuti Iyeyo adzapulumutsa anthu ake ku machimo awo.”
22 Zonsezi zinachitika kukwaniritsa zimene Ambuye ananena mwa mneneri kuti,
23 “Onani namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli,” kutanthauza kuti, “Mulungu ali nafe.”
24 Yosefe atadzuka, anachita zomwe mngelo wa Ambuye uja anamulamulira. Iye anamutenga Mariya kukhala mkazi wake.
25 Koma sanagone malo amodzi mpaka mwanayo atabadwa ndipo anamutcha dzina lake Yesu.
Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.