8Koma kunena za ine, ndadzazidwa ndi mphamvu,ndi Mzimu wa Yehova,ndi kulungama, ndi kulimba mtima,kuti ndilalikire za kugalukira kwa Yakobo,kwa Israeli za tchimo lake.
9Imvani izi, inu atsogoleri a nyumba ya Yakobo,inu olamulira nyumba ya Israeli,inu amene mumadana ndi kuweruza kolungama;ndipo mumakhotetsa zinthu zonse zolondola;
10inu amene mukumanga Ziyoni pokhetsa magazi,ndi Yerusalemu ndi kuyipa kwanu.
12Choncho chifukwa cha inu,Ziyoni adzatipulidwa ngati munda,Yerusalemu adzasanduka bwinja,ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.