6Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa,wamphamvu ndi wosawerengeka;uli ndi mano a mkango,zibwano za mkango waukazi.
7Wawononga mphesa zangandipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu.Wakungunula makungwa akendi kuwataya,kusiya nthambi zake zili mbee.
7
8Lirani ngati namwali wovala chiguduli,chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.
9Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwasizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova.Ansembe akulira,amene amatumikira pamaso pa Yehova.
10Minda yaguga,nthaka yauma;tirigu wawonongeka,vinyo watsopano watha,mitengo ya mafuta yauma.
11Khalani ndi nkhawa, inu alimi,lirani mofuwula inu alimi a mphesa;imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele,pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.
12Mpesa waumandipo mtengo wamkuyu wafota;makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi,mitengo yonse ya mʼmunda yauma.Ndithudi chimwemwe cha anthuchatheratu.
13Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani;lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe.Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse,inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga;pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwasizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.
14Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya,itanani msonkhano wopatulika.Sonkhanitsani akuluakulundi anthu onse okhala mʼdzikoku nyumba ya Yehova Mulungu wanundipo alirire Yehova.
14
15Kalanga ine tsikulo!Pakuti tsiku la Yehova layandikira;lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
15
16Kodi chakudya chathu sichachotsedwaife tikuona?Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathusimulibe chimwemwe ndi chisangalalo?