14Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni;fuwula mokweza, iwe Israeli!Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse,iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!
15Yehova wachotsa chilango chako,wabweza mdani wako.Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako;sudzaopanso chilichonse.
16Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti,“Usaope, iwe Ziyoni;usafowoke.
17Yehova Mulungu wako ali pakati pako,ali ndi mphamvu yopulumutsa.Adzakondwera kwambiri mwa iwe,adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake,adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”
17
18“Ndidzakuchotserani zowawaza pa zikondwerero zoyikika;nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.
20Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani;pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu.Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemupakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansipamene ndidzabwezeretsa mtendere wanuinu mukuona,”akutero Yehova.